13/08/2025
MUKUDZEYI MAKOMBE (JAH PRAYZAH)
Mukudzeyi makombe, mwana wa john ndi shirley, anabadwa pa 4 july 1987 ku nyadire mission ku uzumba ku zimbabwe. Mu banja la ana 5 koma 2 anamwalira. Iye ndi omaliza m'banjamo.
Mu umwana wake. Iye amakonda kulemba ndi kuwerenga ma novel abambo ake. Omwe adali a teacher pa school ina komanso amakonda kusambira ndikusaka nyama(ulenje).
Mukudzeyi adaphunzira pa musamhi primary school ndi musamhi secondary school ku murehwa kenaka adapita ku harare kwa uncle ake komwe adakaphunzira pa sukulu ina.
Zoimba adaziyambira ku school ndipo ankaimba reggae ndi dancehall koma nyimbozi zimangotchuka mu ghetto momwe amakhala. Mukudzeyi adayamba kuimba afro jazz ndi dj thando ndipo adaimba nyimbo ngati "sorry mama". 2007, adatulutsa album yoyamba ya "sungano" kenaka ma album ena awiri. 2013, mukudzeyi adatulutsa album ya chi 4 ya "tsviringo", imene mudali nyimbo ya gotchi gotchi yomwe idakhala song of the year. Mukudzeyi anatchuka kwambiri ndi nyimbo ya "mudhara vachauya" komanso "watora mari". Mukudzeyi waimbapo ndi diamond, mafikizolo,Yemi Alade, oliver mtukudzi ndi davido.
Mukudzeyi amatchedwa JAH PRAYZAH kamba koti dzina lake limatathauza kuti BLESS JAH ndipo iye ankafuna kulowa usilikari koma kamba ka mayi ake, zinakanika ndipo kuyambira pompo, jah prayzah amavala ngati msirikari pamodzi ndi band yake ya 3rd generation. Iye adatenga chilolezo kuchokera ku zimbabwe defence force kuti azivala za usilikari poti ndi ambassador wao.
Jah prayzah adapezeka ndi mlandu wothawa a police ndi azamiseu ku shurungwi kamba koyendetsa galimoto yosalembetsa ya mercedenz benz e320 ndipo adamugwira ku gweru.
Jah prayzah adakwatira rufaro chiwureso, yemwe adabereka naye ana akazi atatu ndi wa mamuna m'modzi.
Mukudzeyi jnr
keana
keyla
kelly
Jah prayzah ndi oyimba oyamba ku zimbabwe kuwina mtv award.
Jah adagwitsa ntchito ndalama zokwana $7000 pa birth day ya mum ake ndipo adagulitsapo cd pa mtengo wa $12000 yomwe ndipafupi fupi k21million.
Kupatula k