18/01/2026
NYENGO MSABATAYI KUYAMBIRA PA 19 JANUARY MPAKA PA 25 JANUARY, 2026.
✓ Kuyambira mawa lolemba pa 19 January mpaka lachiwiri pa 20 January 2026, tiyembekezere nyengo yotentha ndi yamitambo yapatali patali komanso mvula ya mabingu m’madera ochepa, ndipo yamphamvu ikhonza kugwa mmadera ena. Izi zili chonchi kamba ka mphepo zochokera kumpoto chakumvuma.
✓Koma pofika lachitatu, tiyembekezere nyengo ya mphepo, ndi ya mvula yamabingu kudzagwa m’madera ochulukirapo, komabe pali chiopsezo cha ng’amba m’madera ena a mchigwa cha mtsinje wa Shire, Mzimba ndi Karonga.
✓Mphepo zikuyembekezereka kuomba panyanja mwamphanvu nthawi zina maka kuyambira lachitatu.
✓ Mlingo wa mvula yambiri omwe tinalandira unali 155.2mm pa 16 January 2026 kuchokera ku Fort Lister m’boma la Phalombe.
*MALANGIZO M’SABATALI*
● Mvula yamabingu: Tikhale m’malo otetezeka
● Alimi akulimbikitsidwa kutsatira mauthenga a zanyengo kuti azikonzekeretse bwino kunyengo yomwe ili kudza.
© Department of Climate Change and Meteorological Services