Gøxy p

Gøxy p Goxy p

Tsiku Limene Tinaika M’manda Munthu WamoyoGawo 1Sindinalire pa mwambo wamaliro.Anthu onse ankayembekezera kuti ndilire—c...
12/02/2026

Tsiku Limene Tinaika M’manda Munthu Wamoyo

Gawo 1

Sindinalire pa mwambo wamaliro.

Anthu onse ankayembekezera kuti ndilire—chifukwa James ndi ine tinakulira limodzi.

Tinkathamangitsa mbuzi m’mphepete mwa nyanja, tinkaba mango m’mitengo ya anthu ena, ndipo tinkalota maloto ang’onoang’ono ngati mmene achinyamata amachitira moyo ukuwoneka kutali.

Munthu akamwalira, umayenera kulira.
Makamaka akakhaka wamwalirayo ndi wachichepere komanso akakhala kuti anali nzako.

Koma pamene ankatsitsa thupi lake m’manda, chimene ndimamva sichinali chisoni…
Chinali chisokonezo. Chifukwa James samawoneka ngati munthu wakufa.

Nkhope yake inali bata kwambiri, ngati munthu amene wangogona chifukwa chakutopa ndi ulendo wautali. Anamwalira osadwala.

Anangomukulunga m’mphatsa yolimba, kungobisa chifuwa chake, manja ake, mapazi ake. Adzukulu ankagwira ntchito mofulumira.

Mofulumira kwambiri. Panalibe bokosi la maliro. Mphatsa yokha. Panalibe mapepala ochokera kuchipatala osonyeza kuti munthu wamwaliradi.

Ndipo abale ake ochokera kutali sanadikiridwe kuti afike. Samalora munthu kufunsa mafunso.
Nditafunsa mmodzi mwa akuluakulu akubanja chifukwa chimene sitinamutengere James kuchipatala, sanandiyang’ane n'komwe.

Maso awo anangoyang'ana pansi. “Pali Imfa zina,” anatero mwakachetechete, “siziyenera kukhala Nthawi yaitali munthuyo asanaikidwe.”

Mayi wina pafupi nane anangopinda miyendo. Ndipo Wina anatchura dzina langa mwachangu, kundichenjeza kuti ndikhale chete, ndisalankhule ngati ndisakufuna mavuto.

Ndinameza mawu anga. Ndinachita mantha m'malo mwake. Ndipo nyimbo zinayamba—pang’onopang’ono, mosalekeza—zolimbikitsa amoyo, zosokoneza akufa (kwathu sipadziko tingopitilira).

Fumbi linakwera mumlengalenga pamene anthu ankayenda mwachisoni. Dzuwa linali likutentha.

Kenako ndinazizidwa ndi mantha ankulu.

Pamene donthi loyamba linagunda thupi la James… Zala zake zinasutha.
Kamodzi kokha.
Kugwedezeka kochepa.

Mpweya unandithera m’khosi. Ndinatsegula pakamwa panga kuti ndifuule, kuti a

 Apolisi m’boma la Salima amanga a Linda Banwell azaka 33, atapezeka ndi chamba opanda mapepala owayeneleza. Mneneri wa ...
07/02/2026



Apolisi m’boma la Salima amanga a Linda Banwell azaka 33, atapezeka ndi chamba opanda mapepala owayeneleza.

Mneneri wa polisi ya Salima, Sub Inspector Rebecca Ndiwate wati a Banwell awamanga m’bandakucha wa lero pa msika wa Katelera pomwe apolisi adakhazikitsapo malo ochitila chipikisheni.

A Ndiwate ati adagwira a Banwell pomwe amachokera mbali za boma la Nkhotakota, kutsatira kulephera kuwonetsa mapepala owayeneleza kupezeka ndi chambachi.

A Banwell ndiochokera m’mudzi mwa Bango, mfumu yaikulu Mwadzama m’boma la Nkhotakota.

(by Fegson Phabuli-Salima: 02/07/26)

07/02/2026

Source: zodiak

Zodiak Online yapeza kuti ophunzira ena pa sukulu ya sekondale koma yogonera komweko ya Ntchisi auzidwa kuti apite kaye kwao kaamba ka mchitidwe wa ufiti omwe ukuganizilidwa kuti ukuchitika pasukuluyi.

Ena mwa ophunzirawa maka anyamata, auza Zodiak Online kuti kwa nthawi yaitali akhala akumabwebweta, kugwiridwa malo obisika komanso kudinidwa akamagona.

Pakadali pano, mlembi wamkulu mu unduna wa za maphuziro Dr Ken Ndala wapempha nthawi kuti ayankhulepo pa nkhaniyi.

Koma, mu uthenga ojambula omwe mphuzitsi wamkulu pa sukulupo a Alice Donda watulutsa omweso Zodiak Online yakwanitsa kuupeza ukufotokoza kuti ganizo lotumiza ophunzirawa kwao lachitika mogwirizana ndi unduna wamaphuziro.

Malinga ndi uthengawu, ophunzirawa adaopseza kuti ngati saloledwa kupita kaye m'ma kwao aphwanya sukuluyo.

26/01/2026
25/12/2025

Kuipasa hit song yanemwe Achina Gattah Ase

18/12/2025

Abale mulipo

24/01/2024

K Banton ndidolo kwambili

Address

Machinjili
Blantyre

Telephone

+265985978065

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Gøxy p posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Share