29/07/2024
Kampani ya Airtel Malawi yalengeza kuti yakweza thandizo lomwe limapereka ku mpikisano wa Airtel Top 8 Cup kuchoka pa K234 million kwa zaka zitatu kufika pa K655 million kwa zaka zinanso zitatu.
Izi zikutanthauza kuti Mpikisanowu uli pa K98 million ndipo opambana mu 2024 alandira K30 million ndipo othera panambala yachiwiri adzalandira K10 million, pomwe matimu omwe a kutenga nawo gawo alandira K2. 5 million aliyense.
Charles Kamoto, mkulu wakampaniyi waulula izi lero, lolemba, ku Mpira Village mu nzinda wa Blantyre.
Kamoto wati alingalira zokweza thandizo poyang'anira zofuna kuthandiza mtsogoleri wa Football Association of Malawi (FAM), Fleetwood Haiya, pa ngodya zake zofuna kutukula masewerowa m'dziko muno.
Ndipo Haiya wayamikira zomwe kampaniyi yachita pobweranso ndi thandizoli lomwe likhale likuperekedwa kwa zaka zina zitatu.
Iye wati thandizoli likwaniritsa ngodya zake zofuna kusintha kayendesedwe kamasewerowa m'dziko muno.
Source : Timveni Online