18/07/2026
"MUKAWAUZE KUMUDZIKO KUTI NDIKUPULUMUKIRA MANGOWA KUDIMBA KUNO NDIYE MUSAMALIZEMO..."
Amenewa anali mawu afupi, koma olemera ndi ululu. Atangowanena, maso ake anayamba kutseka pang'onopang'ono, mpweya wake unayamba kuchepa, ndipo patangopita mphindi zochepa anapuma komaliza.
Anthu onse amene anali pafupi anangoyamba kulira chifukwa sanamvetse tanthauzo la mawu ake.
Patapita masiku ochepa, anthu a m'banja anayamba kukumbukira kuti nthawi zambiri ankadandaula kuti usiku akamalota amangoona anthu akumuthamangitsa kupita kumunda wina, ndipo ankadzuka ali ndi mantha kwambiri. Koma palibe amene anaganiza kuti zimene ankafotokozazo zinali zomuvutitsa kwambiri m'maganizo mwake.
Tsiku la maliro linafika. Misozi inali yosatha. Mayi ake ankangolira mokweza, "Mwana wanga, unandisiya chifukwa chiyani? Kodi unafuna kundiuza chiyani pa mawu ako omaliza?"
Abambo ake anangokhala chete, maso awo odzaza ndi misonzi. Ana aang'ono a m'banjamo sankamvetsa chifukwa chake munthu amene ankasewera nawo tsiku lililonse sanadzukenso.
Mpando wake unatsala wopanda munthu. Chipinda chake chinangokhala chete. Zovala zake zinali pomwepo, koma mwini wake sanabwerenso.
Panatha miyezi ingapo anthu akupeza zolemba kudimba "MUKAWAUZE KUMUDZIKO KUTI NDIKUPULUMUKIRA MANGOWA KUDIMBA KUNO NDIYE MUSAMALIZEMO..." ndipo anthu am'mudzi anasiya kudya mango amtengo uliwonse mpaka tsiku ndi tsiku mango amachepa mpaka nkufika pokutha onse . Ndipo tsiku lina mango onse atatha anaitanisa nsima yamazira ndipo anthu akubanja anaphikadi ndikupitisa kudimba atavindikira bwino ndipo pobwera m'mawa lake anapeza zakudya zonse zadyedwa mbalenso zavindikiridwa . Ulendo omaliza unali omweyo mpaka pano kuli ziiii kungoti chete ngati bodza.
Nthawi zina imfa imasiya mafunso ambiri kuposa mayankho. Mawu omaliza a munthu amatha kukhala chinsinsi chimene chimakhala m'mitima ya achibale moyo wawo wonse.
Choncho tisamachedwetse kusonyeza chikondi kwa anthu athu.
Tiyeni tizikondana, tizikhululukirana, ndi kupemphererana chifukwa sitikudziwa tsiku kapena nthawi imene tidzanene mawu athu omaliza.
"Pakuti munthu aliyense ali ngati nthunzi; amaoneka kanthawi, kenako n'kusowa."
Moyo ndi waufupi. Konda banja lako, lemekeza anzako, ndipo khala wokonzeka nthawi zonse, chifukwa mawa silinalonjezedwe kwa aliyense. 💔ðŸ˜
Based on true story ! Moto Salumpha